News in English

Mchewa ozungulira mutu yekha ndi yemwe angakonde a Chakwera, Yatero AFORD

Chipani cha Alliance for Democracy (AFORD) chati “ndi m’chewa ozungulira mutu yekha yomwe angavotere a Lazarus Chakwera. Chris Taulo, yemwe ndi mkulu owona zofaritsa nkhani ku chipani cha AFORD, wanena izi pa msokhano wachipanichi la Mulungu ku Mponela m’boma la Dowa. “Ndikubwelezanso kunena kuti ndi Mchewa ozungulira mutu yekha yemwe angakonde a Chakwera pamene nthumba […]

The post Mchewa ozungulira mutu yekha ndi yemwe angakonde a Chakwera, Yatero AFORD appeared first on Malawi Voice.

Under fire

Chipani cha Alliance for Democracy (AFORD) chati “ndi m’chewa ozungulira mutu yekha yomwe angavotere a Lazarus Chakwera.

Chris Taulo, yemwe ndi mkulu owona zofaritsa nkhani ku chipani cha AFORD, wanena izi pa msokhano wachipanichi la Mulungu ku Mponela m’boma la Dowa.

“Ndikubwelezanso kunena kuti ndi Mchewa ozungulira mutu yekha yemwe angakonde a Chakwera pamene nthumba la feteleza lili lodula koopsa, pamene tidamuchotsa munthu wina yemwe amagulitsa nthumba K20, 000….alipo angazikonde zimenezi? Wamisala yekha ndi amene angazikonde zimenezi,” anatero a Taulo pa maso pa mtsogoleri wa chipanichi a Enock Chihana.

Chipani cha AFORD chili mu mgwirizano wa Tonse omwe ukutsogozedwa ndi a Chakwera.

The post Mchewa ozungulira mutu yekha ndi yemwe angakonde a Chakwera, Yatero AFORD appeared first on Malawi Voice.

Читайте на 123ru.net